Mutharika akwiya ndi kumangidwa kwa mamembala a DPP

Mtsogoleri wa chipani cha Democratic Progressive (DPP) a Peter Mutharika ati ndi wokwiya ndi kumangidwa kwa posachedwapa kwa akuluakulu a chipanichi.

“Ndiri ndi chisoni komanso okwiya kwambiri chifukwa anthu akumangidwa popanda chifukwa.

“Ndikupempha abusa a Chakwera kuti boma lanu lisiye nkhaza pozunza a Malawi komanso DPP ndipo m’malo mwake mulimbane ndi njala ndi umphawi m’dziko muno,” atero a Mutharika.

A Mutharika alankhula izi lero kwa Luwanda ku Machinjiri ku Blantyre komwe akuchititsa misokhano yoimaima.

Akuluakulu a chipani cha DPP motsogozedwa ndi a Mutharika, akonza ulendo oyendera anthu m’madera angapo munzinda wa Blantyre kuphatikizapo madera a Mbayani, Chemusa, Ndirande ndi Bangwe.

About Augustine Muwotcha

View all posts by Augustine Muwotcha →

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *